Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 13:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo kodi tidzamvera inu, kucita coipa ici cacikuru conse, kulakwira Mulungu wathu ndi kudzitengera akazi acilendo?

28. Koma wina wa ana a Yoyada, mwana wa Eliasibu mkuru wa ansembe, anali mkamwini wa Sanibalati Mhoroni; cifukwa cace ndinampitikitsa kumcotsa kwa ine.

29. Muwakumbukile Mulungu wanga, popeza anadetsa unsembe, ndi pangano la unsembe, ndi la Alevi.

30. Momwemo ndinawayeretsa kuwacotsera acilendo onse, ndi kuikira udikiro ansembe ndi Alevi, yense ku nchito yace;

31. ndi copereka ca nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukile, Mulungu wanga, cindikomere.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 13