30. Ndipo ansembe ndi Alevi anadziyeretsa okha, nayeretsa anthu, ndi zipata, ndi linga.
31. Pamenepo ndinakwera nao akuru a Yuda pa lingali, ndinaikanso oyamikira magulu awiri akuru oyenda molongosoka; lina loyenda ku dzanja lamanja palinga kumka ku cipata ca kudzala;
32. ndi pambuyo pao anayenda Hosaya, ndi limodzi la magawo awiri a akuru a Yuda,
33. ndi Azariya, Ezara ndi Mesulamu,