Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nahumu 3:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Kumveka kwa cikoti, ndi mkokomo wa kuyenda kwa njinga za magareta; ndi kaphata kaphata wa akavalo, ndi gwegwegwe wa magareta;

3. munthu wokwera pa kavalo, ndi lupanga lonyezimira, ndi mkondo wong'anipa; ndi aunyinji ophedwa, ndi cimulu ca mitembo, palibe kutha zitanda; angokhumudwa ndi zitanda;

4. cifukwa ca ciwerewere cocuruka ca waciwerewere wokongola, ndiye mkaziyo mwini nyanga, wakugulitsa amitundu mwa ciwerewere cace, ndi mabanja mwa nyanga zace.

5. Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndidzaphimba nkhope yako ndi nsaru yako yoyesa mthendene; ndipo ndidzaonetsa amitundu umarisece wako, ndi maufumu manyazi ako.

Werengani mutu wathunthu Nahumu 3