8. Koma ndi cigumula cosefukira adzatha konse malo ace, nadzapitikitsira adani ace kumdima.
9. Mulingaliranji cotsutsana ndi Yehova? Iye adzatha psiti; nsautso siidzauka kawiri.
10. Pakuti cinkana akunga minga yoyangayanga, naledzera naco coledzeretsa cao, adzathedwa konse ngati ciputu couma.