Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nahumu 1:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. KATUNDU wa Nineve. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

2. Yehova ndiye Mulungu wansanje, nabwezera cilango; Yehova ndiye wobwezera cilango, ndi waukali ndithu; Yehova ndiye wobwezera cilango oyambana naye, nasungira mkwiyo pa adani ace.

3. Yehova ndiye wolekerera mkwiyo, koma wa mphamvu yaikuru; ndi wosamasula ndithu woparamula; njira ya Yehova iri m'kabvumvulu ndi mumkuntho; ndipo mitambo ndiyo pfumbi la mapazi ace.

4. Adzudzula nyanja, naiphwetsa, naumitsa mitsinje yonse; Basana ndi Karimeli afota, ndi duwa la ku Lebano linyala.

5. Mapiri agwedezeka cifukwa ca Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pace, ndi maiko ndi onse okhala m'mwemo.

Werengani mutu wathunthu Nahumu 1