Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 9:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. panali mudzi waung'ono muli anthu owerengeka; ndipo inadzako mfumu yaikuru, niizinga ndi nkhondo, nimangapo malinga akuru;

15. koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mudziwo ndi nzeru yace; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.

16. Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ace.

17. Mau a anzeru acete amveka koposa kupfuula kwa wolamulira mwa zitsiru.

18. Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wocimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 9