Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 7:4-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.

5. Kumva cidzudzulo ca anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.

6. Pakuti kuseka kwa citsiru kunga minga irikutetheka pansi pa mphika; icinso ndi cabe.

7. Indetu nsautso iyarutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.

8. Citsiriziro ca kanthu ciposa ciyambi cace; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.

9. Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'cifuwa ca zitsiru.

10. Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.

11. Nzeru iri yabwino pamodzi ndi colowa; akuona dzuwa apindula nayo.

12. Pakuti nzeru icinjiriza monga ndalama zicinjiriza; koma kudziwa kupambana, cifukwa nzeru isunga moyo wa eni ace.

13. Tapenya nchito ya Mulungu; pakuti ndani akhoza kulungamitsa comwe iye anacikhotetsa?

14. Tsiku la mwai kondwera, koma tsiku la tsoka lingirira; Mulungu waika ici pambali pa cinzace, kuti anthu asapeze kanthu ka m'tsogolo mwao.

15. Ndaona zonsezi masiku anga acabe; pali wolungama angofa m'cilungamo cace, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwace.

16. Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?

17. Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?

18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.

19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 7