Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 7:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cisoni ciposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.

4. Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.

5. Kumva cidzudzulo ca anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.

6. Pakuti kuseka kwa citsiru kunga minga irikutetheka pansi pa mphika; icinso ndi cabe.

7. Indetu nsautso iyarutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.

8. Citsiriziro ca kanthu ciposa ciyambi cace; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.

9. Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'cifuwa ca zitsiru.

10. Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 7