Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 7:13-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Tapenya nchito ya Mulungu; pakuti ndani akhoza kulungamitsa comwe iye anacikhotetsa?

14. Tsiku la mwai kondwera, koma tsiku la tsoka lingirira; Mulungu waika ici pambali pa cinzace, kuti anthu asapeze kanthu ka m'tsogolo mwao.

15. Ndaona zonsezi masiku anga acabe; pali wolungama angofa m'cilungamo cace, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwace.

16. Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?

17. Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?

18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.

19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.

20. Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.

21. Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;

22. pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

23. Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.

24. Cakutari ndi cakuyadi adzacipeza ndani?

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 7