Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 5:8-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kucotsa cilungamo ndi ciweruzo mwaciwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkuru wopambana asamalira; ndipo alipo akuru ena oposa amenewo.

9. Phindutu la dziko lipindulira onse; ngakhale mfumu munda umthandiza.

10. Wokonda siliva sadzakhuta siliva; ngakhale wokonda cuma sadzakhuta phindu; icinso ndi cabe.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 5