7. Pakuti monga mu unyinji wa maloto muli zacabe motero mocuruka mau; koma dziopa Mulungu.
8. Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kucotsa cilungamo ndi ciweruzo mwaciwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkuru wopambana asamalira; ndipo alipo akuru ena oposa amenewo.
9. Phindutu la dziko lipindulira onse; ngakhale mfumu munda umthandiza.