Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 4:14-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pakuti aturuka m'nyumba yandende kulowa ufumu; komanso yemwe abadwa m'dziko lace asauka.

15. Ndinapenyera anthu onse amoyo akuyenda kunja kuno, kuti anali ndi mwana, waciwiri, amene adzalowa m'malo mwace.

16. Anthu onse sawerengeka, ngakhale onsewo anawalamulira; koma amene akudza m'mbuyo sadzakondwera naye. Icinso ndi cabe nicisautsa mtima.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 4