Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 3:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kanthu kali konse kali ndi nthawi yace ndi cofuna ciri conse ca pansi pa thambo ciri ndi mphindi yace;

2. mphindi yakubadwa ndi mphindi yakumwalira; mphindi yakubzyala ndi mphindi yakuzula zobzyalazo;

3. mphindi yakupha ndi mphindi yakuciza; mphindi yakupasula ndi mphindi yakumanga;

4. mphindi yakugwa misozi ndi mphindi yakuseka; mphindi yakulira ndi mphindi yakubvina;

5. mphindi yakutaya miyala ndi mphindi yakukundika miyala; mphindi yakufungatirana ndi mphindi yakuleka kufungatirana;

6. mphindi yakufunafuna ndi mphindi yakumwazika; mphindi yakusunga ndi mphindi yakutaya;

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 3