Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 2:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndinati mumtima mwanga, Tiyetu, ndikuyese ndi cimwemwe; tapenya tsono zabwino; ndipo taona, icinso ndi cabe.

2. Ndinati, Kuseka ndi misala; ndi cimwemwe kodi cicita ciani?

3. Ndinafuna mumtima mwanga kusangalatsa thupi langa ndi vinyo, mtima wanga ulikunditsogolera mwanzeru, ndi kugwira utsiru, kuti ndizindikire cabwinoco ca ana a anthu nciani cimene azicicita pansi pa thambo masiku onse a moyo wao.

4. Ndinadzipangira zazikuru; ndinadzimangira nyumba; ndi kunka mipesa;

5. ndinakonza mphanie ndi minda yanga, ndi kuokamo mitengo ya zipatso za mitundu mitundu;

6. ndinadzipangira ndekha matamanda a madzi akuthirira madzi m'nkhalango momeramo mitengo;

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 2