Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 10:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ciyambi ca mau a m'kamwa mwace ndi utsiru; ndipo cimariziro ca m'kamwa mwace ndi misala yoipa,

14. Citsiru cicurukitsanso mau; koma munthu sadziwa cimene cidzaoneka; ndipo ndani angamuuze comwe cidzakhala m'tsogolo mwace?

15. Nchito ya zitsiru izitopetsa zonsezo, pakuti sicidziwa kunka kumudzi.

16. Tsoka kwa dzikowe, pamene mfumu yako ndiye mwana, ndipo akalonga ako adyera mamawa!

17. Mwai kwa dzikowe, pamene mfumu yako ndiye mwana wa aufulu, ndipo akalonga ako adya pa nthawi yoyenera akalimbe osati akaledzere ai.

18. Tsindwi litewa ndi mphwai za eni ace; nyumba nidontha ndi ulesi wa manja.

19. Amaphikira zakudya kuti asekere, vinyo nakondweretsa moyo; ndipo ndalama zibvomera zonse.

20. Usatemberere mfumu ngakhale poganizira; usatemberere wolemera m'cipinda cogona iwemo; pakuti mbalame ya mlengalenga idzanyamula mauwo, ndipo couluka ndi mapiko cidzamveketsa zonenazo.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 10