Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 10:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nchenche zakufa zinunkhitsa moipa nizioletsa mafuta onunkhira a sing'anga; comweco kupusa kwapang'ono kuipitsa iye amene achuka cifukwa ca nzeru ndi ulemu.

2. Wanzeru, mtima wace uli ku dzanja lace lamanja; koma citsiru, mtima wace kulamanzere.

3. Inde, poyendanso citsiru panjira, nzeru yace imthera ndipo angoti kwa onse kuti, Ndine citsiru.

4. Ngati mkuru akukwiyira, usasiye malo ako; cifukwa cifatso cipembedza utacimwa kwambiri.

5. Pali coipa ndaciona pansi pano, ngati kulakwa koyambira ndi mkuru;

6. utsiru ukhazikika pamwamba penipeni, ndipo olemera angokhala mwamanyazi.

7. Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, ndi mafumu, alikuyenda pansi ngati akapolo.

8. Wokumba mbuna adzagwamo; ndipo woboola mpanda njoka idzamluma.

9. Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.

10. Citsulo cikakhala cosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pocenjeza.

11. Njoka ikaluma isanalodzedwe, watsenga saona mphotho.

12. Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga cisomo; koma milomo ya citsiru idzacimeza.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 10