Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 8:4-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndinu ndikuitanani, amuna,Mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.

5. Acibwana inu, cenjerani,Opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;

6. Imvani, pakuti ndikanena zoposa,Ndi zolungama potsegula pakamwa panga,

7. Pakuti m'kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi,Zoipa zinyansa milomo yanga.

8. Mau onse a m'kamwa mwanga alungama;Mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.

9. Onsewo amveka ndi iye amene azindikira;Alungama kwa akupeza nzeru.

10. Landirani mwambo wanga, si siliva ai;Ndi nzeru kopambana ndi golidi wosankhika.

11. Pakuti nzeru iposa ngale,Ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo,

12. Ine Nzeru ndikhala m'kucenjera, ngati m'nyumba yanga;Ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

13. Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.

15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.

16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,

17. Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.

18. Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.

19. Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka;Phindu langa liposa siliva wosankhika.

20. Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,

21. Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.

22. Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.

23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 8