Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 8:20-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,

21. Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.

22. Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.

23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.

24. Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.

25. Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;

26. Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.

27. Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;Pamene analemba pazozama kwete kwete;

28. Polimbitsa Iye thambo la kumwamba,Pokula akasupe a zozama.

29. Poikira nyanja malire ace,Kuti madzi asapitirire pa lamulo lace;Polemba maziko a dziko,

30. Ndinali pa mbali pace ngati mmisiri;Ndinamsekeretsa tsiku ndi tsiku,Ndi kukondwera pamaso pace nthawi zonse;

31. Ndi kukondwera ndi dziko lace lokhalamo anthu,Ndi kusekerera ndi ana a anthu.

32. Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,Ngodala akusunga njira zanga.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 8