Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 8:15-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.

16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,

17. Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.

18. Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.

19. Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka;Phindu langa liposa siliva wosankhika.

20. Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,

21. Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.

22. Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.

23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.

24. Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.

25. Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;

26. Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.

27. Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;Pamene analemba pazozama kwete kwete;

28. Polimbitsa Iye thambo la kumwamba,Pokula akasupe a zozama.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 8