11. Pakuti nzeru iposa ngale,Ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo,
12. Ine Nzeru ndikhala m'kucenjera, ngati m'nyumba yanga;Ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.
13. Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.
14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.
15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.
16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,
17. Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.
18. Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.
19. Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka;Phindu langa liposa siliva wosankhika.
20. Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,