1. Kodi nzeru siitana,Luntha ndi kukweza mau ace?
2. Iima pamwamba pa mtunda,Pa mphambano za makwalala;
3. Pambali pa cipata polowera m'mudzi,Polowa anthu pa makomo ipfuula:
4. Ndinu ndikuitanani, amuna,Mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.
5. Acibwana inu, cenjerani,Opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;
6. Imvani, pakuti ndikanena zoposa,Ndi zolungama potsegula pakamwa panga,
7. Pakuti m'kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi,Zoipa zinyansa milomo yanga.
8. Mau onse a m'kamwa mwanga alungama;Mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.
9. Onsewo amveka ndi iye amene azindikira;Alungama kwa akupeza nzeru.
10. Landirani mwambo wanga, si siliva ai;Ndi nzeru kopambana ndi golidi wosankhika.
11. Pakuti nzeru iposa ngale,Ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo,
12. Ine Nzeru ndikhala m'kucenjera, ngati m'nyumba yanga;Ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.
13. Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.
14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.
15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.
16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,