Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 7:8-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Alikupita pakhwalala pafupi ndi mphambano ya pa mkaziyo,Ndi kuyenda pa njira ya ku nyumba yace;

9. Pa madzulo kuli sisiro,Pakati pa usiku pali mdima,

10. Ndipo taona, mkaziyo anamcingamira,Atabvala zadama wocenjera mtima,

11. Ali wolongolola ndi wosaweruzika,Mapazi ace samakhala m'nyumba mwace.

12. Mwina ali kumakwalala, mwina ali kumabwalo,Nabisalira pa mphambano zonse.

13. Ndipo anagwira mnyamatayo, nampsompsona;Nati kwa iye ndi nkhope yacipongwe,

14. Nsembe za mtendere ziri nane;Lero ndacita zowinda zanga.

15. Cifukwa cace ndaturuka kudzakucingamira,Kudzafunitsa nkhope yako, ndipo ndakupeza.

16. Ndayala zopfunda pakama panga,Nsaru zamangamanga za thonje la ku Aigupto,

17. Ndakapiza pamphasa panga mankhwala onunkhiraA mvunja ndi cisiyo ndi mtanthanyerere.

18. Tiye tikondwere ndi cikondano mpaka mamawa;Tidzisangalatse ndi ciyanjano.

19. Pakuti mwamuna kulibe kwathu,Wapita ulendo wa kutari;

20. Watenga thumba la ndalama m'dzanja lace,Tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21. Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace,Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22. Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa;Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 7