Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 7:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kuti zikucinjirizire kwa mkazi waciwerewere,Kwa mlendo wamkazi wosyasyalika ndi mau ace.

6. Pakuti pa zenera la nyumba yangaNdinapenyera pa made ace;Ndinaona pakati pa acibwana,

7. Ndinazindikira pakati pa ang'onoMnyamata wopanda nzeru,

8. Alikupita pakhwalala pafupi ndi mphambano ya pa mkaziyo,Ndi kuyenda pa njira ya ku nyumba yace;

9. Pa madzulo kuli sisiro,Pakati pa usiku pali mdima,

10. Ndipo taona, mkaziyo anamcingamira,Atabvala zadama wocenjera mtima,

11. Ali wolongolola ndi wosaweruzika,Mapazi ace samakhala m'nyumba mwace.

12. Mwina ali kumakwalala, mwina ali kumabwalo,Nabisalira pa mphambano zonse.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 7