Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 7:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace,Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22. Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa;Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

23. Mpaka mubvi ukapyoza mphafa yace;Amtsata monga mbalame yotamangira msampha;Osadziwa kuti adzaononga moyo wace.

24. Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,Labadirani mau a m'kamwa mwanga.

25. Mtima wako usapatukire ku njira ya mkaziyo,Usasocere m'mayendedwe ace.

26. Pakuti amagwetsa ambiri, atawalasa;Ndipo ophedwa ndi iye acurukadi.

27. Nyumba yace ndiyo njira ya kumanda,Yotsikira ku zipinda za imfa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 7