Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 7:17-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndakapiza pamphasa panga mankhwala onunkhiraA mvunja ndi cisiyo ndi mtanthanyerere.

18. Tiye tikondwere ndi cikondano mpaka mamawa;Tidzisangalatse ndi ciyanjano.

19. Pakuti mwamuna kulibe kwathu,Wapita ulendo wa kutari;

20. Watenga thumba la ndalama m'dzanja lace,Tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21. Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace,Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22. Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa;Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

23. Mpaka mubvi ukapyoza mphafa yace;Amtsata monga mbalame yotamangira msampha;Osadziwa kuti adzaononga moyo wace.

24. Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,Labadirani mau a m'kamwa mwanga.

25. Mtima wako usapatukire ku njira ya mkaziyo,Usasocere m'mayendedwe ace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 7