Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 7:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwananga, sunga mau anga,Ukundike malangizo anga;

2. Sunga malangizo anga, nukhale ndi moyo;Ndi malamulo anga ngati mwana wa diso lako.

3. Uwamange pa zala zako,Uwalembe pamtima pako;

4. Nena kwa nzeru, Ndiwe mlongwanga;Nuche luntha mbale wako.

5. Kuti zikucinjirizire kwa mkazi waciwerewere,Kwa mlendo wamkazi wosyasyalika ndi mau ace.

6. Pakuti pa zenera la nyumba yangaNdinapenyera pa made ace;Ndinaona pakati pa acibwana,

7. Ndinazindikira pakati pa ang'onoMnyamata wopanda nzeru,

8. Alikupita pakhwalala pafupi ndi mphambano ya pa mkaziyo,Ndi kuyenda pa njira ya ku nyumba yace;

9. Pa madzulo kuli sisiro,Pakati pa usiku pali mdima,

10. Ndipo taona, mkaziyo anamcingamira,Atabvala zadama wocenjera mtima,

11. Ali wolongolola ndi wosaweruzika,Mapazi ace samakhala m'nyumba mwace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 7