Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Udzagona mpaka liti, wolesi iwe?Udzauka ku tulo tako liti?

10. Tulo ta pang'ono, kuodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono, ndi kugona;

11. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.

12. Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu;Amayenda ndi m'kamwa mokhota;

13. Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace,Amalankhula ndi zala zace;

14. Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka;Amapikisanitsa anthu.

15. Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka;Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.

16. Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida;Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

17. Maso akunyada, lilime lonama,Ndi manja akupha anthu osacimwa;

18. Mtima woganizira ziwembu zoipa,Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;

19. Mboni yonama yonong'ona mabodza,Ndi wopikisanitsa abale.

20. Mwananga, sunga malangizo a atate wako,Usasiye malamulo a mako;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6