4. Usaone tulo m'maso mwako,Ngakhale kuodzera zikope zako.
5. Dzipulumutse wekha ngati mphoyo ku dzanja la msaki,Ndi mbalame ku dzanja la msodzi.
6. Pita kunyerere, wolesi iwe,Penya njira zao nucenjere;
7. Ziribe mfumu,Ngakhale kapitao, ngakhale mkuru;
8. Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe;Nizituta dzinthu zao m'masika.
9. Udzagona mpaka liti, wolesi iwe?Udzauka ku tulo tako liti?
10. Tulo ta pang'ono, kuodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono, ndi kugona;
11. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.
12. Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu;Amayenda ndi m'kamwa mokhota;
13. Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace,Amalankhula ndi zala zace;
14. Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka;Amapikisanitsa anthu.
15. Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka;Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.
16. Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida;Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa: