29. Comweco wolowa kwa mkazi wa mnzace;Womkhudzayo sadzapulumuka cilango.
30. Anthu sanyoza mbala ikaba,Kuti ikhutitse mtima wace pomva njala;
31. Koma ikapezedwa idzabwezera kasanu ndi kawiri;Idzapereka cuma conse ca m'nyumba yace.
32. Wocita cigololo ndi mkazi alibe nzeru;Wofuna kuononga moyo wace wace ndiye amatero.
33. Adzalasidwa nanyozedwa;Citonzo cace sicidzafafanizidwa.
34. Pakuti nsanje ndiyo ukali wa mwamuna,Ndipo sadzacitira cifundo tsiku lobwezera cilango.
35. Sadzalabadira ciombolo ciri conse,Sadzapembedzeka ngakhale ucurukitsa malipo,