Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:27-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Kodi mwamuna angatenge moto pa cifuwa cace,Osatentha zobvala zace?

28. Pena kodi mwamuna angayende pa makala oyaka,Osapsya mapazi ace?

29. Comweco wolowa kwa mkazi wa mnzace;Womkhudzayo sadzapulumuka cilango.

30. Anthu sanyoza mbala ikaba,Kuti ikhutitse mtima wace pomva njala;

31. Koma ikapezedwa idzabwezera kasanu ndi kawiri;Idzapereka cuma conse ca m'nyumba yace.

32. Wocita cigololo ndi mkazi alibe nzeru;Wofuna kuononga moyo wace wace ndiye amatero.

33. Adzalasidwa nanyozedwa;Citonzo cace sicidzafafanizidwa.

34. Pakuti nsanje ndiyo ukali wa mwamuna,Ndipo sadzacitira cifundo tsiku lobwezera cilango.

35. Sadzalabadira ciombolo ciri conse,Sadzapembedzeka ngakhale ucurukitsa malipo,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6