Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:19-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Mboni yonama yonong'ona mabodza,Ndi wopikisanitsa abale.

20. Mwananga, sunga malangizo a atate wako,Usasiye malamulo a mako;

21. Uwamange pamtima pako osaleka;Uwalunze pakhosi pako.

22. Adzakutsogolera ulikuyenda,Ndi kukudikira uli m'tulo,Ndi kulankhula nawe utauka.

23. Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika;Ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo;

24. Zikucinjiriza kwa mkazi woipa,Ndi ku lilime losyasyalika la mkazi waciwerewere.

25. Asakucititse kaso m'mtima mwako,Asakukole ndi zikope zace.

26. Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama, udzamariza ndi nyenyeswa;Ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengo wapatari.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6