19. Mboni yonama yonong'ona mabodza,Ndi wopikisanitsa abale.
20. Mwananga, sunga malangizo a atate wako,Usasiye malamulo a mako;
21. Uwamange pamtima pako osaleka;Uwalunze pakhosi pako.
22. Adzakutsogolera ulikuyenda,Ndi kukudikira uli m'tulo,Ndi kulankhula nawe utauka.
23. Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika;Ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo;
24. Zikucinjiriza kwa mkazi woipa,Ndi ku lilime losyasyalika la mkazi waciwerewere.
25. Asakucititse kaso m'mtima mwako,Asakukole ndi zikope zace.
26. Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama, udzamariza ndi nyenyeswa;Ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengo wapatari.