Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida;Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

17. Maso akunyada, lilime lonama,Ndi manja akupha anthu osacimwa;

18. Mtima woganizira ziwembu zoipa,Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;

19. Mboni yonama yonong'ona mabodza,Ndi wopikisanitsa abale.

20. Mwananga, sunga malangizo a atate wako,Usasiye malamulo a mako;

21. Uwamange pamtima pako osaleka;Uwalunze pakhosi pako.

22. Adzakutsogolera ulikuyenda,Ndi kukudikira uli m'tulo,Ndi kulankhula nawe utauka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6