Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:11-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.

12. Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu;Amayenda ndi m'kamwa mokhota;

13. Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace,Amalankhula ndi zala zace;

14. Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka;Amapikisanitsa anthu.

15. Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka;Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.

16. Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida;Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

17. Maso akunyada, lilime lonama,Ndi manja akupha anthu osacimwa;

18. Mtima woganizira ziwembu zoipa,Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;

19. Mboni yonama yonong'ona mabodza,Ndi wopikisanitsa abale.

20. Mwananga, sunga malangizo a atate wako,Usasiye malamulo a mako;

21. Uwamange pamtima pako osaleka;Uwalunze pakhosi pako.

22. Adzakutsogolera ulikuyenda,Ndi kukudikira uli m'tulo,Ndi kulankhula nawe utauka.

23. Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika;Ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo;

24. Zikucinjiriza kwa mkazi woipa,Ndi ku lilime losyasyalika la mkazi waciwerewere.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6