11. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.
12. Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu;Amayenda ndi m'kamwa mokhota;
13. Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace,Amalankhula ndi zala zace;
14. Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka;Amapikisanitsa anthu.
15. Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka;Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.
16. Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida;Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:
17. Maso akunyada, lilime lonama,Ndi manja akupha anthu osacimwa;
18. Mtima woganizira ziwembu zoipa,Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;