Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 6:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwananga, ngati waperekera mnzako cikole,Ngati wapangana kulipirira mlendo,

2. Wakodwa ndi mau a m'kamwa mwako,Wagwidwa ndi mau a m'kamwa mwako.

3. Cita ici tsono; mwananga, nudzipulumutse;Popeza walowa m'dzanja la mnzako,Pita nudzicepetse, numdandaulire mnzako,

4. Usaone tulo m'maso mwako,Ngakhale kuodzera zikope zako.

5. Dzipulumutse wekha ngati mphoyo ku dzanja la msaki,Ndi mbalame ku dzanja la msodzi.

6. Pita kunyerere, wolesi iwe,Penya njira zao nucenjere;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 6