6. Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.
7. Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.
8. Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo,Osayandikira ku khomo la nyumba yace;
9. Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,Ndi zaka zako kwa ankhanza;
10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;
11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;
12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;
13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!
14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.
15. Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.
16. Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?
17. Ikhale ya iwe wekha,Si ya alendo okhala nawe ai.
18. Adalitsike kasupe wako;Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.
19. Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo,Maere ace akukwanire nthawi zonse;Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.
20. Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere,Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?