Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 5:5-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mayendedwe ace atsikira kuimfa;Mapazi ace aumirira kumanda;

6. Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.

7. Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.

8. Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo,Osayandikira ku khomo la nyumba yace;

9. Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,Ndi zaka zako kwa ankhanza;

10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;

11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;

12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;

13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 5