2. Ukasunge zolingalira,Milomo yako ilabadire zomwe udziwa.
3. Pakuti milomo ya mkazi waciwerewere ikukha uci;M'kamwa mwace muti see koposa mafuta.
4. Cimariziro cace ncowawa ngati civumulo,Ndi cakuthwa ngati lupanga lakuthwa konse konse.
5. Mayendedwe ace atsikira kuimfa;Mapazi ace aumirira kumanda;
6. Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.
7. Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.
8. Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo,Osayandikira ku khomo la nyumba yace;
9. Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,Ndi zaka zako kwa ankhanza;
10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;
11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;