Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 5:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

17. Ikhale ya iwe wekha,Si ya alendo okhala nawe ai.

18. Adalitsike kasupe wako;Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19. Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo,Maere ace akukwanire nthawi zonse;Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.

20. Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere,Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?

Werengani mutu wathunthu Miyambi 5