12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;
13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!
14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.
15. Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.
16. Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?
17. Ikhale ya iwe wekha,Si ya alendo okhala nawe ai.
18. Adalitsike kasupe wako;Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.
19. Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo,Maere ace akukwanire nthawi zonse;Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.