Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 5:10-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;

11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;

12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;

13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15. Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

16. Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

17. Ikhale ya iwe wekha,Si ya alendo okhala nawe ai.

18. Adalitsike kasupe wako;Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19. Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo,Maere ace akukwanire nthawi zonse;Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.

20. Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere,Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?

21. Pakuti njira za munthu ziri pamaso pa Yehova,Asinkhasinkha za mayendedwe ace onse.

22. Zoipazacezacezidzagwira woipa;Adzamangidwa ndi zingwe za ucimo wace.

23. Adzafa posowa mwambo;Adzasocera popusa kwambiri.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 5