Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 5:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;

11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;

12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;

13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15. Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 5