10. Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;
11. Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;
12. Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;
13. Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga;Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!
14. Ndikadakhala m'zoipa zonse,M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.
15. Imwa madzi a m'citsime mwako,Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.