Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 5:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwananga, mvera nzeru yanga;Cherera makutu ku luntha langa;

2. Ukasunge zolingalira,Milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

3. Pakuti milomo ya mkazi waciwerewere ikukha uci;M'kamwa mwace muti see koposa mafuta.

4. Cimariziro cace ncowawa ngati civumulo,Ndi cakuthwa ngati lupanga lakuthwa konse konse.

5. Mayendedwe ace atsikira kuimfa;Mapazi ace aumirira kumanda;

6. Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.

7. Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 5