8. Uilemekeze, ndipo idzakukweza;Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.
9. Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;Idzakupatsa korona wokongola.
10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.
11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.
12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.
13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.
14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.
15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.
16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.
17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.
18. Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.
19. Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,