Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 4:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Uilemekeze, ndipo idzakukweza;Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9. Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;Idzakupatsa korona wokongola.

10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.

11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.

13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.

15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.

16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.

17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.

18. Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.

19. Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 4