Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 4:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Mwananga, tamvera mau anga;Cherera makutu ku zonena zanga.

21. Asacoke ku maso ako;Uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22. Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,Nalamitsa thupi lao lonse.

23. Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;Pakuti magwero a moyo aturukamo.

24. Tasiya m'kamwa mokhota,Uike patari milomo yopotoka.

25. Maso ako ayang'ane m'tsogolo,Zikope zako zipenye moongoka,

26. Sinkasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako;Njira zako zonse zikonzeke.

27. Usapatuke ku dzanja lamanja kapena kulamanzere;Suntha phazi lako kusiya zoipa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 4