15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.
16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.
17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.
18. Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.
19. Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,
20. Mwananga, tamvera mau anga;Cherera makutu ku zonena zanga.
21. Asacoke ku maso ako;Uwasunge m'kati mwa mtima wako.
22. Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,Nalamitsa thupi lao lonse.