Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 4:14-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.

15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.

16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.

17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.

18. Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.

19. Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,

20. Mwananga, tamvera mau anga;Cherera makutu ku zonena zanga.

21. Asacoke ku maso ako;Uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22. Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,Nalamitsa thupi lao lonse.

23. Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;Pakuti magwero a moyo aturukamo.

24. Tasiya m'kamwa mokhota,Uike patari milomo yopotoka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 4