1. Ananu, mverani mwambo wa atate,Nimuchere makutu mukadziwe luntha;
2. Pakuti ndikuphunzitsani zabwino;Musasiye cilangizo canga.
3. Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,Wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabala wina.
4. Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,Mtima wako uumirire mau anga;Sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.
5. Tenga nzeru, tenga luntha;Usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;
6. Usasiye nzeru, ndipo Idzakusunga;Uikonde, idzakucinjiriza.