Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 31:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Tsegula pakamwa pako,Nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.

10. Mkazi wangwiro ndani angampeze?Pakuti mtengo wace uposa ngale.

11. Mtima wa mwamuna wace umkhulupirira,Sadzasowa phindu.

12. Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa,Masiku onse a moyo wace.

13. Afuna ubweya ndi thonje,Nacita mofunitsa ndi manja ace.

14. Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.

15. Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.

16. Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.

17. Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,

18. Azindikira kuti malonda ace ampindulira;Nyali yace sizima usiku.

19. Agwira njinga ya thonje ndi dzanja lace,Nafumbata mtengo wace.

20. Aolowera cikhato cace osauka;Natambasulira aumphawi manja ace.

21. Saopera banja lace cipale cofewa;Pakuti banja lace lonse libvala mlangali.

22. Adzipangira zimbwi zamaangamaanga;Nabvala bafuta ndi guta woti biriwiri.

23. Mwamuna wace adziwika kubwalo,Pokhala pakati pa akuru a dziko.

24. Asoka maraya abafuta, nawagulitsa;Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 31