Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 31:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Tsegula pakamwa pako, ukanenere wosalankhula,Ndi mlandu wa amasiye onse.

9. Tsegula pakamwa pako,Nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.

10. Mkazi wangwiro ndani angampeze?Pakuti mtengo wace uposa ngale.

11. Mtima wa mwamuna wace umkhulupirira,Sadzasowa phindu.

12. Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa,Masiku onse a moyo wace.

13. Afuna ubweya ndi thonje,Nacita mofunitsa ndi manja ace.

14. Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 31